Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Hoseya 5:12 - Buku Lopatulika

Ndipo ndikhala kwa Efuremu ngati njenjete, ndi kwa nyumba ya Yuda ngati chivundi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo ndikhala kwa Efuremu ngati njenjete, ndi kwa nyumba ya Yuda ngati chivundi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nchifukwa chake ndidzaononga Efuremu, monga momwe njenjete zimaonongera nsalu, ndidzakhala ngati chilonda choola pa anthu a ku Yuda.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.

Onani mutuwo



Hoseya 5:12
8 Mawu Ofanana  

Momwemo munthu akutha ngati chinthu choola, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.


Pamene mulanga munthu ndi zomdzudzula chifukwa cha mphulupulu, mukanganula kukongola kwake monga mumachita ndi njenjete. Indedi, munthu aliyense ali chabe.


Mkazi wodekha ndiye korona wa mwamuna wake; koma wochititsa manyazi akunga chovunditsa mafupa a mwamunayo.


Chifukwa chake monga ngati lilime la moto likutha chiputu, ndi monga udzu wouma ugwa pansi m'malawi, momwemo muzu wao udzakhala monga wovunda, maluwa ao adzauluka m'mwamba ngati fumbi; chifukwa kuti iwo akana chilamulo cha Yehova wa makamu, nanyoza mau a Woyera wa Israele.


Taonani, Ambuye Yehova adzathandiza Ine; ndani amene adzanditsutsa? Taonani, iwo onse adzatha ngati chovala, njenjete zidzawadya.


Pakuti njenjete idzawadya ngati chofunda, ndi mbozi zidzawadya ngati ubweya; koma chilungamo changa chidzakhala kunthawi zonse, ndi chipulumutso changa kumibadwo yonse.


Koma Mulungu anauikira mphanzi pakucha m'mawa mwake, ndiyo inadya msatsi, nufota.