Ndipo mutu wanga ukadzikweza, mundisaka ngati mkango; mubweranso ndi kudzionetsera modabwitsa kwa ine.
Hoseya 13:7 - Buku Lopatulika Chifukwa chake ndikhala nao ngati mkango; ngati nyalugwe ndidzalalira kunjira. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Chifukwa chake ndikhala nao ngati mkango; ngati nyalugwe ndidzalalira kunjira. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Motero ndidzaŵalumphira ngati mkango, ndidzaŵalalira ngati kambuku m'mbali mwa njira. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Motero ndidzawalumphira ngati mkango, ndidzawabisalira mu msewu ngati kambuku. |
Ndipo mutu wanga ukadzikweza, mundisaka ngati mkango; mubweranso ndi kudzionetsera modabwitsa kwa ine.
Yehova adzatuluka ngati munthu wamphamvu; adzautsa nsanje ngati munthu wa nkhondo; Iye adzafuula, inde adzakuwa zolimba; adzachita zamphamvu pa adani ake.
Wasiya ngaka yake, monga mkango; pakuti dziko lao lasanduka chizizwitso chifukwa cha ukali wa lupanga losautsa, ndi chifukwa cha mkwiyo wake waukali.
Chifukwa chake mkango wotuluka m'nkhalango udzawapha, ndi mmbulu wa madzulo udzawafunkha, nyalugwe adzakhalira m'mizinda mwao, onse amene atulukamo adzamwetulidwa; pakuti zolakwa zili zambiri, ndi mabwerero ao achuluka.
Pakuti ndidzakhala kwa Efuremu ngati mkango, ndi kwa nyumba ya Yuda ngati msona wa mkango; ndidzamwetula Ine ndi kuchoka; ndidzanyamula, ndipo palibe wakulanditsa.
Ndipo anati, Yehova adzadzuma ali mu Ziyoni, nadzamveketsa mau ake ali mu Yerusalemu; podyetsa abusa padzachita chisoni, ndi mutu wa Karimele udzauma.
Kodi mkango udzabangula m'nkhalango wosakhala nayo nyama? Kodi msona wa mkango udzalira m'ngaka mwake usanagwire kanthu?
Ndipo chilombo ndinachionacho chinafanana ndi nyalugwe, ndi mapazi ake ngati mapazi a chimbalangondo, ndi pakamwa pake ngati pakamwa pa mkango; ndipo chinjoka chinampatsa iye mphamvu yake, ndi mpando wachifumu wake, ndi ulamuliro waukulu.