Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 8:17 - Buku Lopatulika

Tulutsa pamodzi ndi iwe zamoyo zonse zili ndi iwe za nyama zonse, zouluka, ndi zinyama, ndi zokwawa zonse zakukwawa padziko lapansi; kuti ziswane padziko lapansi, zibalane, zichuluke padziko lapansi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Tulutsa pamodzi ndi iwe zamoyo zonse zili ndi iwe za nyama zonse, zouluka, ndi zinyama, ndi zokwawa zonse zakukwawa pa dziko lapansi; kuti ziswane pa dziko lapansi, zibalane, zichuluke pa dziko lapansi, zibalane, zichuluke pa dziko lapansi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwezo, mbalame, nyama ndi zokwaŵa, kuti ziswane ndi kubalalika pa dziko lonse lapansi.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwe, mbalame, nyama ndi zokwawa zonse kuti ziswane ndi kuchulukana pa dziko lapansi.”

Onani mutuwo



Genesis 8:17
10 Mawu Ofanana  

Mulungu ndipo anadalitsa zimenezo, nati, Zibalane, zichuluke, zidzaze madzi a m'nyanja, ndi mbalame zichuluke padziko lapansi.


Mulungu ndipo anadalitsa iwo, ndipo adati kwa iwo, Mubalane, muchuluke, mudzaze dziko lapansi, muligonjetse: mulamulire pansomba za m'nyanja, ndi pambalame za m'mlengalenga, ndi pazamoyo zonse zokwawa padziko lapansi.


Tulukamoni m'chingalawamo, iwe ndi ana ako, ndi mkazi wako, ndi akazi a ana ako pamodzi ndi iwe.


Ndipo anatuluka Nowa ndi ana ake, ndi mkazi wake, ndi akazi a ana ake, pamodzi naye:


Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake, nati kwa iwo, Mubalane, muchuluke, mudzaze dziko lapansi.


Ndi inu, mubalane, muchuluke; muswane padziko lapansi, nimuchuluke m'menemo.


Ndipo awadalitsa, kotero kuti achuluka kwambiri; osachepsanso zoweta zao.