Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 44:4 - Buku Lopatulika

Atatuluka m'mzinda asanamuke patali, Yosefe anati kwa tsanyumba wake, Tanyamuka, talondola anthu aja, ukawapeza unene nao, Chifukwa chanji mwabwezera zoipa m'malo mwa zabwino?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Atatuluka m'mudzi asanamuke patali, Yosefe anati kwa tsanyumba wake, Tanyamuka, talondola anthu aja, ukawapeza unene nao, Chifukwa chanji mwabwezera zoipa m'malo mwa zabwino?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Atangoyenda pang'ono kuchoka mumzindamo, Yosefe adauza wantchito wake wamkulu uja kuti, “Nyamuka, uthamangire anthu aja. Ukaŵapeza, uŵafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoipa kwa zabwino?

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Atangotuluka mu mzinda muja, koma asanapite patali, Yosefe anati kwa wantchito wake, “Nyamuka atsatire anthu aja msanga. Ndipo ukawapeza, uwafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoyipa ndi zabwino?

Onani mutuwo



Genesis 44:4
9 Mawu Ofanana  

ndipo anang'amba zovala zao, nasenzetsa yense bulu wake, nabwera kumzinda.


Pamene kudacha, anamukitsa anthu iwo ndi abulu ao.


tapenyani, m'mene atibwezera, kudzatiinga m'cholowa chanu, chimene munatipatsa chikhale cholowa chathu.


Ndipo anandisenza choipa m'malo mwa chokoma, ndi udani m'malo mwa chikondi changa.


Andibwezera choipa m'malo mwa chokoma, inde, asaukitsa moyo wanga.


Wobwezera zabwino zoipa, zoipa sizidzamchokera kwao.


Yesu anayankha iwo, Ndakuonetsani inu ntchito zabwino zambiri za kwa Atate; chifukwa cha ntchito yiti ya izo mundiponya miyala?


Ndipo kunali, atatha kufa amuna onse ankhondo mwa anthu,


Nati kwa Davide, Iwe ndiwe wolungama woposa ine; popeza unandibwezera zabwino, koma ine ndinakubwezera zoipa.