Ndipo Yakobo anafika ndi mtendere kumzinda wa Sekemu umene uli m'dziko la Kanani, pamene anachokera ku Padanaramu; namanga tsasa pandunji pa mzindapo.
Genesis 37:12 - Buku Lopatulika Ndipo abale ake ananka kukaweta zoweta za atate wao mu Sekemu. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ndipo abale ake ananka kukaweta zoweta za atate wao m'Sekemu. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Tsiku lina abale ake a Yosefe adapita ku Sekemu kukaŵeta nkhosa za bambo wao. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Tsono abale ake anapita kukadyetsa ziweto za abambo awo ku Sekemu, |
Ndipo Yakobo anafika ndi mtendere kumzinda wa Sekemu umene uli m'dziko la Kanani, pamene anachokera ku Padanaramu; namanga tsasa pandunji pa mzindapo.
Ndipo abale ake anamchitira iye nsanje, koma atate wake anasunga mau amene m'mtima mwake.
Ndipo Israele anati kwa Yosefe, Kodi abale ako sadyetsa zoweta mu Sekemu? Tiyeni, ndikutuma iwe kwa iwo. Ndipo anati, Ndine pano.
Mudzati, Akapolo anu akhala oweta ng'ombe chiyambire ubwana wathu kufikira tsopano, ife ndi atate athu; kuti mukhale m'dziko la Goseni; chifukwa abusa onse anyansira Aejipito.
anadza anthu ochokera ku Sekemu, ndi ku Silo, ndi ku Samariya, anthu makumi asanu ndi atatu, atameta ndevu zao, atang'amba zovala zao, atadzitematema, anatenga nsembe zaufa ndi lubani m'manja mwao, kunka nazo kunyumba ya Yehova.