Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 36:12 - Buku Lopatulika

Ndipo Timna anali mkazi wake wamng'ono wa Elifazi mwana wamwamuna wa Esau; ndipo anambalira Elifazi Amaleke: amenewa ndi ana aamuna a Ada mkazi wake wa Esau.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Timna anali mkazi wake wamng'ono wa Elifazi mwana wamwamuna wa Esau; ndipo anambalira Elifazi Amaleke: amenewa ndi ana amuna a Ada mkazi wake wa Esau.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

(Timna anali mzikazi wa Elifazi mwana wa Esau, ndipo mwa Timnayo Elifazi adaberekamo Amaleke.) Ameneŵa ndiwo ana a Ada mkazi wa Esau.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Timna anali mzikazi wa Elifazi, mwana wa Esau. Iyeyo anaberekera Elifazi mwana dzina lake Amaleki. Amenewa ndiwo zidzukulu za Ada, mkazi wa Esau.

Onani mutuwo



Genesis 36:12
10 Mawu Ofanana  

Ndipo anabwera nafika ku Enimisipati (kumeneko ndi ku Kadesi), nakantha dziko lonse la Aamaleke, ndiponso Aamori amene akhala mu Hazazoni-Tamara.


Ndipo ana aamuna a Elifazi ndiwo Temani, Omara, Zefo ndi Gatamu, ndi Kenazi.


Ndi ana aamuna a Reuwele: Nahati, ndi Zera, Sama, ndi Miza; amenewa ndi ana a Basemati mkazi wake wa Esau.


Ndi ana a Lotani anali Hori ndi Hemani: mlongo wake wa Lotani anali Timna.


Ana a Elifazi: Temani, ndi Omara, Zefi, ndi Gatamu, Kenazi, ndi Timna, ndi Amaleke.


Musamanyansidwa naye Mwedomu, popeza ndiye mbale wanu; musamanyansidwa naye Mwejipito, popeza munali alendo m'dziko lake.