Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 29:8 - Buku Lopatulika

Ndipo anati, Sitingathe, koma zitasonkhana ziweto zonse, ndipo atagubuduza mwala kuuchotsa pakamwa pa chitsime ndiko; pamenepo ndipo tizimwetsa nkhosa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anati, Sitingathe, koma zitasonkhana ziweto zonse, ndipo atagubuduza mwala kuuchotsa pakamwa pa chitsime ndiko; pamenepo ndipo tizimwetsa nkhosa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Iwo aja adayankha kuti, “Sitingathe kutero mpaka nkhosa zonse zitasonkhana pamodzi, ndipo mwala wa pamwamba pa chitsimewo titaukunkhuniza. Apo tingathe kuzipatsa madzi nkhosazo.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iwo anayankha, “Ayi sitingatero. Tidikira mpaka nkhosa zonse zisonkhane. Zikatero, tigubuduza mwalawu kuwuchotsa pamwamba pa chitsimepo, kenaka nʼkuzimwetsa madzi nkhosazo.”

Onani mutuwo



Genesis 29:8
8 Mawu Ofanana  

Kumeneko ndipo zinasonkhana zoweta zonse: ndipo anagubuduza mwala kuuchotsa pakamwa pa chitsime, namwetsa nkhosa, naikanso mwala pakamwa pa chitsime pamalo pake.


Ndipo iye anati, Taonani, kukali msana, si nthawi yosonkhanitsa zoweta; mwetsani nkhosa, pitani, kadyetseni.


Ali chilankhulire nao, anafika Rakele ndi nkhosa za atate wake, chifukwa anaziweta.


nati kwa iwo, Sitingathe kuchita ichi, kupereka mlongo wathu kwa mwamuna wosadulidwa; chifukwa kumeneko ndiko kutichepetsa ife.


Ndipo anamuikira iye chake pa yekha, ndi iwo chao pa okha, ndi Aejipito akudya naye chao pa okha; chifukwa Aejipito sanathei kudya chakudya pamodzi ndi Ahebri: chifukwa kuchita chomwecho nkunyansira Aejipito.


Ndipo analikunena mwa okha, Adzatikunkhunizira ndani mwalawo, pakhomo la manda?


Ndipo anapeza mwala unakunkhunizidwa kuuchotsa pamanda.


Pakukwera kumzindako anapeza anthu aakazi alikutuluka kuti akatunge madzi, nanena nao, Mlauliyo alipo kodi?