Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 26:20 - Buku Lopatulika

Ndipo abusa a Gerari anakangana ndi abusa a Isaki kuti, Madzi ndi athu; ndipo anatcha dzina la chitsimecho Eseke: chifukwa anakangana naye.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo abusa a Gerari anakangana ndi abusa a Isaki kuti, Madzi ndi athu; ndipo anatcha dzina la chitsimecho Eseke: chifukwa anakangana naye.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma abusa a ku Gerari adayamba kukangana ndi abusa a Isaki, ankati, “Madziŵa ndi athu.” Motero chitsimecho Isaki adachitcha Mkangano, chifukwa adakangana naye.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma abusa a ku Gerari anakangana ndi abusa a Isake nati, “Madziwa ndi athu.” Motero iye anachitcha chitsimecho Mkangano chifukwa anakangana naye.

Onani mutuwo



Genesis 26:20
5 Mawu Ofanana  

Ndipo panali ndeu, abusa a Abramu kudana ndi abusa a Loti. Akanani ndi Aperizi ndipo analinkukhala nthawi yomweyo m'dzikomo.


Ndipo Abrahamu anamdzudzula Abimeleki chifukwa cha chitsime cha madzi, anyamata ake a Abimeleki anachilanda.


Ndipo anyamata a Isaki anakumba m'chigwa, napeza kumeneko chitsime cha madzi otumphuka.


Ndipo anakumbanso chitsime china, ndipo anakangana nachonso; natcha dzina lake Sitina.


Mudzati, Akapolo anu akhala oweta ng'ombe chiyambire ubwana wathu kufikira tsopano, ife ndi atate athu; kuti mukhale m'dziko la Goseni; chifukwa abusa onse anyansira Aejipito.