Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 24:52 - Buku Lopatulika

Ndipo panali pamene anamva mauwo mnyamata wa Abrahamu, anamgwadira Yehova pansi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo panali pamene anamva mauwo mnyamata wa Abrahamu, anamgwadira Yehova pansi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Wantchito wa Abrahamu uja atamva mau ao aja, adaŵeramitsa mutu napembedza Chauta.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Wantchito wa Abrahamu uja atamva zimene anawerama pansi pamaso pa Yehova.

Onani mutuwo



Genesis 24:52
12 Mawu Ofanana  

Munthuyo ndipo anawerama mutu namyamika Yehova.


Ndipo ndinawerama mutu wanga ndi kulambira Yehova, ndi kumyamikira Yehova, Mulungu wa mbuyanga Abrahamu, amene ananditsogolera ine m'njira yakuona, kuti ndikamtengere mwana wamwamuna wake mwana wa mkazi wa mphwake wa mbuyanga.


Taonani, Rebeka ali pamaso pako, mtenge ndi kumuka, akhale mkazi wa mwana wa mbuyako, monga wanena Yehova.


Ndipo Davide anati kwa khamu lonse, Mulemekeze tsono Yehova Mulungu wanu. Ndi khamu lonse linalemekeza Yehova Mulungu wa makolo ao, nawerama, nalambira Yehova, ndi mfumu.


Ndipo Yehosafati anawerama mutu wake, nkhope yake pansi; ndi Ayuda onse, ndi okhala mu Yerusalemu anagwa pansi pamaso pa Yehova, nalambira Yehova.


Tiyeni, tipembedze tiwerame; tigwade pamaso pa Yehova, amene anatilenga.


Ndipo pofika kunyumba anaona kamwanako ndi Maria amake, ndipo anagwa pansi namgwadira Iye; namasula chuma chao, nampatsa Iye mitulo, ndiyo golide ndi lubani ndi mure.


chifukwa chake inenso ndinampereka kwa Yehova; masiku onse a moyo wake aperekedwa kwa Yehova. Ndipo analambira Yehova pomwepo.