Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 24:47 - Buku Lopatulika

Ndipo ndinamfunsa iye kuti, Ndiwe mwana wa yani kodi? Ndipo anati, Ndine mwana wa Betuele, mwana wa Nahori amene anambalira iye Milika: ndipo ndinaika mphete pambuyo pake ndi zingwinjiri pa manja ake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo ndinamfunsa iye kuti, Ndiwe mwana wa yani kodi? Ndipo anati, Ndine mwana wa Betuele, mwana wa Nahori amene anambalira iye Milika: ndipo ndinaika mphete pambuyo pake ndi zingwinjiri pa manja ake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndiye ndinamufunsa kuti, ‘Atate ako ndani?’ Iye anandiyankha kuti, ‘Atate anga ndi Betuele, mwana wa Nahori, amene adamubalira Milika.’ Pamenepo ndinamuveka chipini pa mphuno, ndiponso zigwinjiri pa mikono.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Ndinamufunsa kuti, ‘Ndiwe mwana wa yani?’ “Iye anati, ‘Ndine mwana wa Betueli mwana wa Nahori, amene Milika anamuberekera.’ “Tsono ndinayika chipini pa mphuno yake ndi kumveka zibangiri mʼmikono yake,

Onani mutuwo



Genesis 24:47
9 Mawu Ofanana  

Ndipo mnyamatayo anatulutsa zokometsera zasiliva ndi zagolide, ndi zovala, nampatsa Rebeka: ndipo anapatsa za mtengo wapatali kwa mlongo wake ndi amake.


Mwa omveka anu muli ana aakazi a mafumu; ku dzanja lanu lamanja aima mkazi wa mfumu wovala golide wa ku Ofiri.


Monga chipini chagolide m'mphuno ya nkhumba, momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.


mphete, ndi zipini;