Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 21:27 - Buku Lopatulika

Ndipo Abrahamu anatenga nkhosa ndi ng'ombe, nampatsa Abimeleki, ndipo anapangana pangano onse awiriwo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Abrahamu anatenga nkhosa ndi ng'ombe, nampatsa Abimeleki, ndipo anapangana pangano onse awiriwo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Abrahamu adapatsa Abimeleki nkhosa ndi ng'ombe, ndipo onse aŵiriwo adachita chipangano.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Choncho Abrahamu anabweretsa nkhosa ndi ngʼombe nazipereka kwa Abimeleki, ndipo anthu awiriwo anachita pangano.

Onani mutuwo



Genesis 21:27
15 Mawu Ofanana  

Ndipo anadza wina amene anapulumuka namuuza Abramu Muhebri; ndipo iye analinkukhala pa mitengo yathundu ya pa Mamure Mwamori, mkulu wake wa Esikolo, ndi mkulu wake wa Anere; amenewo ndiwo opangana naye Abramu.


Ndipo anati Abimeleki, Sindinadziwe amene anachita icho; ndipo iwe sunandiuze ine, ndiponso sindinamve koma lero lino.


Ndipo Abrahamu anapatula anaankhosa aakazi asanu ndi awiri pa okha.


Tsopano tiyeni tipangane pangano, ine ndi iwe; likhale mboni pakati pa ine ndi iwe.


Wolandira chokometsera mlandu achiyesa ngale; paliponse popita iye achenjera.


Mtulo wa munthu umtsegulira njira, numfikitsa pamaso pa akulu.


Woyanjana ndi ambiri angodziononga; koma lilipo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.


Mphatso ya m'tseri ipembedza mkwiyo, ndi mtulo wa pamfunga ukali wolimba.


Koma mfulu aganizira zaufulu, nakhazikika m'zaufulu zomwe.


ndipo inatenga wa mbumba yachifumu, nkuchita naye pangano, nkumlumbiritsa, nkuchotsa amphamvu a m'dziko;


opanda nzeru, osasunga mapangano, opanda chikondi cha chibadwidwe, opanda chifundo;


Abale, ndinena monga munthu. Pangano, lingakhale la munthu, litalunzika, palibe munthu aliyesa chabe, kapena kuonjezapo.


Pamenepo Yonatani ndi Davide anapangana pangano, pakuti adamkonda iye ngati moyo wa iye yekha.