Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 19:32 - Buku Lopatulika

tiyeni, timwetse atate vinyo, tidzagona naye, kuti tisunge mbeu za atate wathu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

tiyeni, timwetse atate vinyo, tidzagona naye, kuti tisunge mbeu za atate wathu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tiye tiŵaledzeretse abamboŵa kuti agone nafe, kuti mtundu usathe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tiye tiwamwetse vinyo ndipo tigone nawo. Tikatero mtundu wathu udzakhalapobe.”

Onani mutuwo



Genesis 19:32
8 Mawu Ofanana  

Ndipo ananenana wina ndi wina, Tiyeni tipange njerwa, tiziotchetse. Ndipo anali ndi njerwa naziyesa miyala, ndi katondo anayesa matope.


Ndipo anamwetsa atate wao vinyo usiku womwewo; woyamba ndipo analowa nagona naye atate wake; ndipo sanadziwe pomwe anagona ndi pomwe anauka.


namwa vinyo wake, naledzera; ndipo anali wamaliseche m'kati mwa hema wake.


Mphunzitsi, Mose anatilembera, kuti, Akafa mbale wake wa munthu, nasiya mkazi, wosasiya mwana, mbale wake atenge mkazi wake, namuukitsire mbale wakeyo mbeu.


Koma mudziyang'anire nokha, kuti kapena mitima yanu ingalemetsedwe ndi madyaidya ndi kuledzera, ndi zosamalira za moyo uno, ndi kuti tsiku ilo lingafikire inu modzidzimutsa ngati msampha;