Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Genesis 11:32 - Buku Lopatulika

Masiku a Tera anali zaka mazana awiri kudza zisanu; ndipo anafa Tera mu Harani.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Masiku a Tera anali zaka mazana awiri kudza zisanu; ndipo anafa Tera m'Harani.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndipo Tera adafera kumeneko ali wa zaka 205.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tera anamwalira ku Harani ali ndi zaka 205.

Onani mutuwo



Genesis 11:32
6 Mawu Ofanana  

Ndipo Tera anatenga Abramu mwana wake wamwamuna, ndi Loti mwana wa Harani, mwana wake wamwamuna, ndi Sarai mpongozi wake, mkazi wa mwana wake Abramu; ndipo anatuluka pamodzi nao ku Uri wa kwa Akaldeya kuti amuke ku dziko la Kanani, ndipo anafika ku Harani, nakhala kumeneko.


Ndipo Yehova anati kwa Abramu, Tuluka iwe m'dziko lako, ndi kwa abale ako, ndi kunyumba ya atate wako, kunka ku dziko limene ndidzakusonyeza iwe;


Ndipo mnyamatayo anatenga ngamira khumi za mbuyake, namuka: chifukwa kuti chuma chonse cha mbuyake chinali m'dzanja lake: ndipo anachoka namuka ku Mesopotamiya, kumzinda wa Nahori.


Kodi milungu ya amitundu inawalanditsa amene makolo anga anawaononga, ndiwo Gozani, ndi Harani Rezefe, ndi ana a Edeni okhala mu Telasara?


Ndipo zitatha izi, Yobu anakhala ndi moyo zaka zana limodzi mphambu makumi anai, naona ana ake ndi zidzukulu zake mibadwo inai.


Kodi milungu ya amitundu yaipulumutsa iyo, imene atate anga anaipasula? Gozani ndi Harani ndi Rezefe ndi ana a Edeni amene anali mu Telasara.