Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 33:6 - Buku Lopatulika

Ndipo ana a Israele anazichotsera zokometsera zao kuyambira paphiri la Horebu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo ana a Israele anazichotsera zokometsera zao kuyambira pa phiri la Horebu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Motero kuyambira ku phiri lija la Horebu, Aisraele sadavalenso zokongoletsa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kotero Aisraeli anavula zodzikometsera zawo pa phiri la Horebu.

Onani mutuwo



Eksodo 33:6
7 Mawu Ofanana  

Koma Mose analikuweta gulu la Yetero mpongozi wake, wansembe wa ku Midiyani; natsogolera gululo m'tsogolo mwa chipululu, nafika kuphiri la Mulungu, ku Horebu.


Ndipo anthu onse anathyola mphete zagolide zinali m'makutu mwao, nabwera nazo kwa Aroni


Ndipo pamene anthu anamva mau awa oipa anachita chisoni; ndipo panalibe mmodzi anavala zokometsera zake.


Ndipo Yehova anati kwa Mose, Nena ndi ana a Israele, Inu ndinu anthu opulupudza; ndikakwera kulowa pakati pa inu kamphindi kamodzi, ndidzakuthani; koma tsopano, vulani zokometsera zanu, kuti ndidziwe chomwe ndikuchitireni.


Ndipo Mose akatenga chihemacho nachimanga kunja kwa chigono, kutali kwa chigono; nachitcha, Chihema chokomanako. Ndipo kunakhala kuti yense wakufuna Yehova anatuluka kunka ku chihema chokomanako kunja kwa chigono.


Choipa chako chidzakulanga iwe, mabwerero ako adzakudzudzula iwe; dziwa, nuone, kuti ichi ndi choipa ndi chowawa, kuti wasiya Yehova Mulungu wako, ndi kuti kundiopa Ine sikuli mwa iwe, ati Ambuye, Yehova wa makamu.


Ndipo anthu a Ninive anakhulupirira Mulungu, nalalikira chosala, navala chiguduli, kuyambira wamkulu kufikira wamng'ono wa iwowa.