Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 33:23 - Buku Lopatulika

ndipo pamene ndichotsa dzanja langa udzaona m'mbuyo mwanga; koma nkhope yanga siidzaoneka.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

ndipo pamene ndichotsa dzanja langa udzaona m'mbuyo mwanga; koma nkhope yanga siidzaoneka.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kenaka ndichotsa dzanja langa, ndipo undiwona kumsana, koma nkhope yanga suiwona ai.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kenaka ine ndidzachotsa dzanja langa ndipo iwe udzaona msana wanga, koma nkhope yanga sidzaoneka.”

Onani mutuwo



Eksodo 33:23
6 Mawu Ofanana  

Kodi ukhoza kupeza Mulungu mwa mufunafuna? Ukhoza kupeza Wamphamvuyonse motsindika?


Taonani, awa ndi malekezero a njira zake; ndi chimene tikumva za Iye ndi chinong'onezo chaching'ono; koma kugunda kwa mphamvu yake akuzindikiritsa ndani?


Ananenanso, Sungathe kuona nkhope yanga; pakuti palibe munthu adzandiona Ine ndi kukhala ndi moyo.


Kulibe munthu anaona Mulungu nthawi zonse; Mwana wobadwa yekha wakukhala pa chifuwa cha Atate, Iyeyu anafotokozera.


Pakuti tsopano tipenya m'kalirole, ngati chimbuuzi; koma pomwepo maso ndi maso. Tsopano ndizindikira mderamdera; koma pomwepo ndidzazindikiratu, monganso ndazindikiridwa.


amene Iye yekha ali nao moyo wosatha, wakukhala m'kuunika kosakhozeka kufikako; amene munthu sanamuone, kapena sangathe kumuona; kwa Iye kukhale ulemu ndi mphamvu yosatha. Amen.