Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 29:32 - Buku Lopatulika

Ndipo Aroni ndi ana ake aamuna adye nyama ya nkhosa yamphongoyo, ndi mkate uli mudengu, pa khomo la chihema chokomanako.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Aroni ndi ana ake amuna adye nyama ya nkhosa yamphongoyo, ndi mkate uli mudengu, pa khomo la chihema chokomanako.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndipo Aroni ndi ana akewo adye nyama ya nkhosa yamphongoyo, pamodzi ndi buledi wam'lichero uja pakhomo pa chihema chamsonkhano.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aaroni ndi ana ake adye nyama ya nkhosa yayimunayi pamodzi ndi buledi amene ali mʼdengu pa khomo la tenti ya msonkhano.

Onani mutuwo



Eksodo 29:32
8 Mawu Ofanana  

ndi mkate wamphumphu umodzi, ndi kamtanda ka mkate wosakaniza ndi mafuta, ndi kamtanda kamodzi kaphanthi, zili mu dengu la mkate wopanda chotupitsa wokhala pamaso pa Yehova;


Ndipo utenge nkhosa yamphongo yodzaza manja, nuphike nyama yake m'malo opatulika.


Ndipo adye zimene anachita nazo choteteza, kuti awadzaze manja ndi kuwapatulitsa; koma mlendo asadyeko, pakuti nzopatulika izi.


Ndipo Mose anati kwa Aroni ndi kwa ana ake aamuna, Phikani nyamayi pakhomo pa chihema chokomanako; ndipo muidyere komweko ndi mkate uli mu dengu la nsembe zodzaza manja, monga ndinauza, ndi kuti, Aroni ndi ana ake aidye.


Kuti analowa m'nyumba ya Mulungu, nadya mikate yoonetsa, imene yosaloleka kudya iye kapena amene anali naye, koma ansembe okhaokha.