Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 29:19 - Buku Lopatulika

Ndipo utenge nkhosa yamphongo yinayo; ndi Aroni ndi ana ake aamuna aike manja ao pamutu pa nkhosa yamphongoyo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo utenge nkhosa yamphongo yinayo; ndi Aroni ndi ana ake amuna aike manja ao pamutu pa nkhosa yamphongoyo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Tsono utenge nkhosa yamphongo inayo. Aroni ndi ana ake aamuna asanjike manja ao pamutu pa nkhosayo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Utenge nkhosa yayimuna ina ndipo Aaroni ndi ana ake aamuna asanjike manja awo pamutu pake.

Onani mutuwo



Eksodo 29:19
5 Mawu Ofanana  

Pamenepo uiphe nkhosa yamphongoyo, nutapeko pa mwazi wake, ndi kuupaka pa ndewerere ya khutu lamanja la Aroni, ndi pa ndewerere ya khutu lamanja ana ake aamuna, ndi pa chala chachikulu cha dzanja lao lamanja, ndi pa chala chachikulu cha phazi lao lamanja ndi kuuwaza mwaziwo paguwa la nsembe posungulira.


Ndipo uziike mu dengu limodzi, ndi kubwera nazo mudengu, pamodzi ndi ng'ombe yamphongo ndi nkhosa ziwiri zamphongo.


Ndipo aike dzanja lake pamutu pa nsembe yopsereza; ndipo idzalandiridwa m'malo mwake, imtetezere.


Ndipo aike dzanja lake pamutu wa chopereka chake, ndi kuipha pa chipata cha chihema chokomanako; ndipo ana a Aroni, ansembewo, awaze mwazi wake paguwa la nsembe pozungulira.