Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 28:28 - Buku Lopatulika

Ndipo amange chapachifuwa pa mphete zake ndi mphete za efodi ndi mkuzi wamadzi, kuti chikhale pa mpango wa efodi; ndi kuti chapachifuwa chisamasuke paefodi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo amange chapachifuwa pa mphete zake ndi mphete za efodi ndi mkuzi wamadzi, kuti chikhale pa mpango wa efodi; ndi kuti chapachifuwa chisamasuke paefodi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono ulumikize mphete za chovala chapachifuwacho ku mphete za chovala cha efodi chija ndi kamkuzi kobiriŵira, kuti chovala chapachifuwacho chikhale pamwamba pa lamba wolukidwa mwaluso uja, ndipo chovala chapachifuwa chilumikizike bwino ku chovala cha efodi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tsono umangirire mphete za pa chovala chapachifuwa zija ku mphete za efodi ndi chingwe chamtundu wa mtambo, kulumikiza lamba ndi chovala chapachifuwacho kuti chovala chapachifuwacho chisalekane ndi efodi.

Onani mutuwo



Eksodo 28:28
9 Mawu Ofanana  

miyala yaberulo, ndi miyala yoika paefodi, ndi pachapachifuwa.


Upangenso mphete ziwiri zagolide, ndi kuzimanga pa zapamapewa ziwiri za efodi, m'munsi, ku mbali yake ya kutsogolo, pafupi pa msoko wake, pamwamba pa mpango wa efodi.


Ndipo Aroni azinyamula maina a ana a Israele pa chapachifuwa cha chiweruzo pamtima pake, pakulowa iye m'malo opatulika, akhale chikumbutso pankhope pa Yehova kosalekeza.


Ndipo uombe mwinjiro wa efodi ndi lamadzi lokha.


Nuchiike pamkuzi wamadzi, ndipo chikhale panduwira, chikhale patsogolo pake pa nduwira.


Ndipo mpango wa efodi, wokhala pamenepo, kuti ammange nao, ukhale wa chiombedwe chomwecho, ndi woombera kumodzi, wagolide, ndi thonje lamadzi, ndi lofiirira ndi lofiira, ndi bafuta wa thonje losansitsa.


zovala zokoma za kutumikira nazo m'malo opatulika, ndi zovala zopatulika za Aroni wansembe, ndi zovala za ana ake, kuchita nazo ntchito ya nsembe.


Nena ndi ana a Israele, nuwauze kuti adziombere mphonje m'mphepete mwa zovala zao, mwa mibadwo yao, naike pamphonje m'mphepetemo thonje lamadzi.