Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 22:26 - Buku Lopatulika

Ukati ulandire chikole kaya chovala cha mnansi wako, koma polowa dzuwa uchibwezere kwa iye;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ukati ulandire chikole kaya chovala cha mnansi wako, koma polowa dzuwa uchibwezere kwa iye;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mukatenga mwinjiro wa munthu wina ngati chigwiriro kuti adzakulipireni, muubweze dzuŵa lisanaloŵe,

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mukatenga chovala cha mnzanu kuti chikhale chikole mumubwezere dzuwa lisanalowe

Onani mutuwo



Eksodo 22:26
16 Mawu Ofanana  

Pakuti wamtenga chikole kwa mbale wako wopanda chifukwa, ndi kuvula ausiwa zovala zao.


Akankhizira kwao bulu wa amasiye, atenga ng'ombe ya mfedwa ikhale chikole.


Agona amaliseche usiku wonse opanda chovala, alibe chofunda pachisanu.


Akwatula wamasiye kubere, natenga chikole chovala cha osauka;


M'mwemo anafikitsa kwa Iye kufuula kwa osauka; ndipo anamva Iye kufuula kwa ozunzika.


Mwapenya; pakuti mumayang'anira chivutitso ndi chisoni kuti achipereke m'manja mwanu; waumphawi adzipereka kwa Inu; wamasiye mumakhala mthandizi wake.


Mngelo wa Yehova azinga kuwatchinjiriza iwo akuopa Iye, nawalanditsa iwo.


Tenga malaya a woperekera mlendo chikole; woperekera mkazi wachilendo chikole umgwire mwini.


Ngati ulibe chobwezera kodi achotserenji kama lako pansi pako?


kapena kusautsa wina aliyense, wosatenga chigwiriro, wosatenga zofunkha; koma anapatsa wanjala chakudya chake, naveka wamaliseche ndi chovala,


wosasautsa munthu aliyense, koma wambwezera wangongole chigwiriro chake, wosatenga zofunkha, anampatsa wanjala chakudya chake, naveka wamaliseche ndi chovala,


woipayo akabweza chikole, nakabweza icho anachilanda mwachifwamba, nakayenda m'malemba a moyo wosachita chosalungama, adzakhala ndi moyo ndithu, sadzafa.


nagona pansi pa zofunda za chikole kumaguwa a nsembe ali onse, ndi m'nyumba ya Mulungu wao akumwa vinyo wa iwo olipitsidwa.


Musamaipsa mlandu wa mlendo, kapena wa ana amasiye; kapena kutenga chikole chovala cha mkazi wamasiye;


Munthu asalandire chikole mphero, ngakhale mwanamphero, popeza alandirapo chikole moyo wa munthu.