Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 21:30 - Buku Lopatulika

Akamuikira dipo, azipereka chiombolo cha moyo wake monga mwa zonse adamuikira.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Akamuikira dipo, azipereka chiombolo cha moyo wake monga mwa zonse adamuikira.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma ngati amlamula kuti adziwombole, adzayenera kulipira ndalama, kuti apulumutse moyo wake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma ngati wauzidwa kuti alipire, iye apereke zimene wauzidwazo kuti awombole moyo wake.

Onani mutuwo



Eksodo 21:30
6 Mawu Ofanana  

Akayambana amuna, nakakantha mkazi ali ndi pakati, kotero kuti abala, koma alibe kuphwetekwa; alipe ndithu, monga momwe amtchulira mwamuna wa mkaziyo; apereke monga anena oweruza.


Koma ngati ng'ombe ikatunga masiku adapitawo, ndipo anamchenjeza mwiniyo, koma osaisunga iye, ndipo ikapha mwamuna kapena mkazi, aiponye miyala ng'ombeyo, ndi mwini wakeyo amuphenso.


Ingakhale yatunga mwana wamwamuna kapena wamkazi, aichitire monga mwa chiweruzo ichi.


Pamene uwerenga ana a Israele, monga mwa mawerengedwe ao, munthu yense apereke kwa Yehova chiombolo cha pa moyo wake, pa kuwerengedwa iwowa; kuti pasakhale mliri pakati pao, pakuwerengedwa iwowa.


Chiombolo cha moyo wa munthu ndicho chuma chake; koma wosauka samva chidzudzulo.