Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Eksodo 21:17 - Buku Lopatulika

Munthu wakutemberera atate wake, kapena amai wake, aphedwe ndithu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Munthu wakutemberera atate wake, kapena amai wake, aphedwe ndithu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Munthu aliyense wotemberera bambo wake kapena mai wake, aphedwe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.

Onani mutuwo



Eksodo 21:17
11 Mawu Ofanana  

Uzilemekeza atate wako ndi amai ako; kuti achuluke masiku ako m'dziko limene Yehova Mulungu wako akupatsa iwe.


Akalimbana amuna, ndipo wina akakantha mnzake ndi mwala, kapena ndi nkhonya, wosafa iye, koma wakhulungira pakama;


Wotemberera atate wake ndi amake, nyali yake idzazima mu mdima woti bii.


Pali mbadwo wotemberera atate ao, osadalitsa amai ao.


Diso lochitira atate wake chiphwete, ndi kunyoza kumvera amake, makwangwala a kumtsinje adzalikolowola, ana a mphungu adzalidya.


Munthu akakhala naye mwana wamwamuna wopulukira, ndi wopikisana naye, wosamvera mau a atate wake, kapena mau a mai wake, wosawamvera angakhale anamlanga;


Pamenepo amuna onse a mzinda wake amponye miyala kuti afe; chotero muchotse choipacho pakati panu; ndipo Israele wonse adzamva, nadzaopa.


Wotembereredwa iye wakupeputsa atate wake kapena mai wake. Ndi anthu onse anene, Amen.