Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Ahebri 8:7 - Buku Lopatulika

Pakuti loyamba lija likadakhala lopanda chilema sakadafuna malo a lachiwirilo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti loyamba lija likadakhala lopanda chilema sakadafuna malo a lachiwirilo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chipangano choyamba chija chikadakhala changwiro, sipakadafunikanso china m'malo mwake.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ngati pangano loyamba lija likanakhala langwiro, sipakanafunikanso lina mʼmalo mwake.

Onani mutuwo



Ahebri 8:7
5 Mawu Ofanana  

Pamenepo kodi chilamulo chitsutsana nao malonjezano a Mulungu? Msatero ai. Pakuti chikadapatsidwa chilamulo chakukhoza kuchitira moyo, chilungamo chikadachokera ndithu kulamulo.


Koma sindichita chipangano ichi ndi lumbiro ili ndi inu nokha;


Ndipo pakadakhala ungwiro mwa unsembe wa Chilevi (pakuti momwemo anthu analandira chilamulo), pakadatsala kusowa kotani kuti auke wansembe wina monga mwa dongosolo la Melkizedeki, wosayesedwa monga mwa dongosolo la Aroni?


Pakutitu kuli kutaya kwake kwa lamulo lidadza kalelo, chifukwa cha kufooka kwake, ndi kusapindulitsa kwake,


Koma tsopano Iye walandira chitumikiro chomveka koposa, umonso ali Nkhoswe ya pangano labwino loposa, limene likhazikika pa malonjezano oposa.