Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Ahebri 7:21 - Buku Lopatulika

koma Iye ndi lumbiro mwa Iye amene anenana kwa Iye, Walumbira Ambuye ndipo sadzalapa, iwe ndiwe wansembe nthawi yosatha).

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

koma Iye ndi lumbiro mwa Iye amene anenana kwa Iye, Walumbira Ambuye ndipo sadzalapa, iwe ndiwe wansembe nthawi yosatha).

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma Yesu adaloŵa unsembe wake ndi lumbiro, pamene Mulungu adamuuza kuti, “Ambuye adalumbira, ndipo sadzasintha maganizo ake akuti, ndiwe wansembe mpaka muyaya.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma Yesu ankakhala wansembe ndi lumbiro pamene Mulungu anati, “Ambuye analumbira ndipo sangasinthe maganizo ake, ‘Iwe ndi wansembe wamuyaya.’ ”

Onani mutuwo



Ahebri 7:21
10 Mawu Ofanana  

Yehova walumbira, ndipo sadzasintha, Inu ndinu wansembe kosatha monga mwa chilongosoko cha Melkizedeki.


Mulungu sindiye munthu, kuti aname; kapena mwana wa munthu, kuti aleke; kodi anena, osachita?


Pakuti mphatso zake ndi kuitana kwake kwa Mulungu sizilapika.


Monga anenanso mwina, Iwe ndiwe wansembe wa nthawi zonse monga mwa dongosolo la Melkizedeki.


pakuti amchitira umboni, Iwe ndiwe wansembe nthawi yosatha monga mwa dongosolo la Melkizedeki.


Ndipo monga momwe sikudachitike kopanda lumbiro; (pakuti iwotu anayesedwa ansembe kopanda lumbiro;


Ndipo iwo ndiwo ambiri anakhala ansembe, popeza imfa idawaletsa asakhalebe;


Pakuti chilamulo chimaika akulu a ansembe anthu, okhala nacho chifooko; koma mau a lumbirolo, amene anafika chitapita chilamulo, aika Mwana, woyesedwa wopanda chilema kunthawi zonse.


Ndiponso Wamphamvu wa Israele sanama kapena kulapa; popeza Iye sali munthu kuti akalapa.