Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Ahebri 3:11 - Buku Lopatulika

Monga ndinalumbira mu ukali wanga: Ngati adzalowa mpumulo wanga!

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Monga ndinalumbira m'ukali wanga: Ngati adzalowa mpumulo wanga!

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Motero ndili wokwiya ndidalumbira kuti, ‘Sadzaloŵa konse mu mpumulo umene ndidaŵakonzera.’ ”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kotero Ine ndinalumbira nditakwiya kuti, ‘Iwo sadzalowa mu mpumulo wanga.’ ”

Onani mutuwo



Ahebri 3:11
13 Mawu Ofanana  

Potero anawasamulira dzanja lake, kuti awagwetse m'chipululu:


Chifukwa chake ndinalumbira mu mkwiyo wanga, ngati adzalowa mpumulo wanga.


Koma Aamaleke ndi Akanani akhala m'chigwamo; tembenukani mawa, nimunke ulendo wanu kuchipululu, njira ya ku Nyanja Yofiira.


Ine Yehova ndanena, ndidzachitira ndithu ichi khamu ili lonse loipa lakusonkhana kutsutsana nane; adzatha m'chipululu muno, nadzafamo.


Ndipo masiku amene tinayenda kuchokera ku Kadesi-Baranea, kufikira tidaoloka mtsinje wa Zeredi, ndiwo zaka makumi atatu mphambu zisanu ndi zitatu; kufikira utatha mbadwo wonse wa amuna ankhondo m'chigono, monga Yehova adawalumbirira.


Popeza ife amene takhulupirira tilowa mpumulowo, monga momwe ananena, Monga ndalumbira mu mkwiyo wanga, ngati adzalowa mpumulo wanga. Zingakhale ntchitozo zidatsirizika kuyambira kuzika kwa dziko lapansi.


Ndipo m'menemonso, Ngati adzalowa mpumulo wanga.


Momwemo utsalira mpumulo wa Sabata wa kwa anthu a Mulungu.