Ahebri 2:16 - Buku Lopatulika Pakuti ndithu salandira angelo, koma alandira mbeu ya Abrahamu. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Pakuti ndithu salandira angelo, koma alandira mbeu ya Abrahamu. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Paja nchodziŵikiratu kuti sadatekeseke ndi angelo ai koma ndi zidzukulu za Abrahamu. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Pakuti tikudziwanso kuti sathandiza angelo, koma zidzukulu za Abrahamu. |
Pakuti inde mdulidwe uli wabwino, ngati iwe umachita lamulo; koma ngati uli wolakwira lamulo, mdulidwe wako wasanduka kusadulidwa.
Ndipo malonjezano ananenedwa kwa Abrahamu ndi kwa mbeu yake. Sanena, Ndipo kwa zimbeu, ngati kunena zambiri; komatu ngati kunena imodzi, Ndipo kwa mbeu yako, ndiye Khristu.
Pakutitu iwo anatilanga masiku owerengeka monga kudawakomera; koma Iye atero, kukatipindulitsa, kuti tikalandirane nao pa chiyero chake.
nakamasule iwo onse amene, chifukwa cha kuopa imfa, m'moyo wao wonse adamangidwa ukapolo.
Potero kudamuyenera kufanizidwa ndi abale m'zonse, kuti akadzakhala mkulu wa ansembe wachifundo ndi wokhulupirika m'zinthu za kwa Mulungu, kuti apereke dipo la zoipa za anthu.
Pakuti anthu amalumbira pa wamkulu; ndipo m'chitsutsano chao chilichonse lumbiro litsiriza kutsimikiza.
amene anazindikirikatu lisanakhazikike dziko lapansi, koma anaonetsedwa pa chitsiriziro cha nthawi,