Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Ahebri 13:1 - Buku Lopatulika

Chikondi cha pa abale chikhalebe.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Chikondi cha pa abale chikhalebe.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pitirizani kukondana monga abale.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pitirizani kukondana monga abale.

Onani mutuwo



Ahebri 13:1
30 Mawu Ofanana  

Onani, nkokoma ndi kokondweretsa ndithu kuti abale akhale pamodzi!


Zinthu izi ndilamula inu, kuti mukondane wina ndi mnzake.


Ndipo pakufika tsiku la Pentekoste, anali onse pamodzi pamalo amodzi.


Ndipo unyinji wa iwo akukhulupirira anali wa mtima umodzi ndi moyo umodzi; ndipo sananene mmodzi kuti kanthu ka chuma anali nacho ndi kake ka iye yekha; koma anali nazo zonse zodyerana.


Pakuti adakuitanani inu, abale, mukhale mfulu; chokhacho musachite nao ufulu wanu chothandizira thupi, komatu mwachikondi chitiranani ukapolo.


Koma chipatso cha Mzimu ndicho chikondi, chimwemwe, mtendere, kuleza mtima, chifundo, kukoma mtima, chikhulupiriro,


Pakuti mwa Khristu Yesu kapena mdulidwe kapena kusadulidwa kulibe mphamvu; komatu chikhulupiriro, chakuchititsa mwa chikondi.


ndi kusamalitsa kusunga umodzi wa Mzimu mwa chimangiriro cha mtendere.


ndipo yendani m'chikondi monganso Khristu anakukondani inu, nadzipereka yekha m'malo mwathu, chopereka ndi nsembe kwa Mulungu, ikhale fungo lonunkhira bwino.


Tiziyamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu, abale, monga kuyenera; pakuti chikhulupiriro chanu chikula chikulire, ndipo chichulukira chikondano cha inu nonse, yense pa mnzake;


ndipo tiganizirane wina ndi mnzake kuti tifulumizane ku chikondano ndi ntchito zabwino,


Popeza mwayeretsa moyo wanu pakumvera choonadi kuti mukakonde abale ndi chikondi chosanyenga, mukondane kwenikweni kuchokera kumtima;


Chitirani ulemu anthu onse. Kondani abale. Opani Mulungu, Chitirani mfumu ulemu.


Chotsalira, khalani nonse a mtima umodzi, ochitirana chifundo, okondana ndi abale, achisoni, odzichepetsa;


koposa zonse mukhale nacho chikondano chenicheni mwa inu nokha; pakuti chikondano chikwiriritsa unyinji wa machimo;


ndi pachipembedzo chikondi cha pa abale; ndi pachikondi cha pa abale chikondi.


Ndipo lamulo lake ndi ili, kuti tikhulupirire dzina la Mwana wake Yesu Khristu, ndi kukondana wina ndi mnzake monga anatilamulira.


Munthu akati, kuti, Ndikonda Mulungu, nadana naye mbale wake, ali wabodza: pakuti iye wosakonda mbale wake amene wamuona, sangathe kukonda Mulungu amene sanamuone.


Koma ndili nako kanthu kotsutsana ndi iwe, kuti unataya chikondi chako choyamba.