Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Ahebri 12:12 - Buku Lopatulika

Mwa ichi limbitsani manja ogooka, ndi maondo olobodoka;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mwa ichi limbitsani manja ogooka, ndi maondo olobodoka;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Limbitsani tsono manja anu ofooka ndiponso maondo anu agooka.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nʼchifukwa chake limbitsani manja anu otopa ndi mawondo anu ogowoka.

Onani mutuwo



Ahebri 12:12
11 Mawu Ofanana  

Mabondo anga agwedezeka chifukwa cha kusala; ndi mnofu wanga waonda posowa mafuta.


Limbitsani manja opanda mphamvu, ndi kulimbitsa maondo a gwedegwede.


Ndipo kudzakhala akanena ndi iwe, Uusa moyo chifukwa ninji? Uzikati, Chifukwa cha mbiri; pakuti ikudza, ndi mtima uliwonse udzasungunuka, ndi manja onse adzalenda, ndi mzimu uliwonse udzakomoka, ndi maondo onse adzaweyeseka ngati madzi; taona ilinkudza, inde idzachitika, ati Ambuye Yehova.


Manja onse adzalenda, ndi maondo onse adzaweyeseka ngati madzi.


Pamenepo padasandulika pa nkhope pake pa mfumu, ndi maganizo ake anamsautsa, ndi mfundo za m'chuuno mwake zinaguluka, ndi maondo ake anaombana.


Ndiye mopanda kanthu mwakemo ndi mwachabe, ndi wopasuka; ndi mtima usungunuka, ndi maondo aombana, ndi m'zuuno zonse muwawa, ndi nkhope zao zatumbuluka.


Tsiku lomwelo adzati kwa Yerusalemu, Usaopa Ziyoni, manja anu asakhale olefuka.


Koma tidandaulira inu abale, yambirirani amphwayi, limbikitsani amantha mtima. Chirikizani ofooka, mukhale oleza mtima pa onse.


Pakuti talingirirani Iye amene adapirira ndi ochimwa otsutsana naye kotere, kuti mungaleme ndi kukomoka m'moyo mwanu.


ndipo mwaiwala dandauliro limene linena nanu monga ndi ana, Mwana wanga, usayese chopepuka kulanga kwa Ambuye, kapena usakomoke podzudzulidwa ndi Iye;