Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Yohane 1:8 - Buku Lopatulika

Mudzipenyerere nokha, kuti mungataye zimene tazichita, koma kuti mulandire mphotho yokwanira.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mudzipenyerere nokha, kuti mungataye zimene tazichita, koma kuti mulandire mphotho yokwanira.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma yesetsani kuti mukalandire mphotho yathunthu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chenjerani kuti mungataye chimene mwagwirira ntchito, koma chitani khama kuti mukalandire mphotho yanu yonse.

Onani mutuwo



2 Yohane 1:8
20 Mawu Ofanana  

Ndipo aphunzitsi adzawala ngati kunyezimira kwa thambo; ndi iwo otembenuza ambiri atsate chilungamo ngati nyenyezi kunthawi za nthawi.


Ndipo Yesu anayankha nati kwa iwo, Yang'anirani, asasokeretse inu munthu.


Koma yang'anirani; onani ndakuuziranitu zinthu zonse, zisanafike.


Koma inu mudziyang'anire inu nokha; pakuti adzakuperekani inu ku bwalo la akulu a milandu; ndipo adzakukwapulani m'masunagoge; ndipo pamaso pa akazembe ndi mafumu mudzaimirira chifukwa cha Ine, kukhale umboni kwa iwo.


Ndipo anati kwa iyenso, Khala iwenso woweruza mizinda isanu.


Ndipo Iye anati, Yang'anirani musasocheretsedwe; pakuti ambiri adzadza m'dzina langa, nadzanena, Ndine amene; ndipo, Nthawi yayandikira; musawatsate pambuyo pao.


Wakumweta alandira kulipira, nasonkhanitsira chobala kumoyo wosatha; kuti wofesayo akakondwere pamodzi ndi womwetayo.


ndipo potsiriza pake pa onse, anaoneka kwa inenso monga mtayo.


Ngati ntchito ya munthu aliyense ikhala imene anaimangako, adzalandira mphotho.


Koma wookayo ndi wothirirayo ali amodzi; koma yense adzalandira mphotho yake ya iye yekha, monga mwa kuchititsa kwake kwa iye yekha.


Kodi mudamva zowawa zambiri zotere kwachabe? Ngatitu kwachabe.


Ndiopera inu, kuti kapena ndadzivutitsa ndi inu chabe.


chokhachi, kumene tidafikirako, mayendedwe athu alinganeko.


Koma tadzikumbutsani masiku akale, m'menemo mutaunikidwa mudapirira chitsutsano chachikulu cha zowawa;


Potero musataye kulimbika kwanu, kumene kuli nacho chobwezera mphotho chachikulu.


ndi kuyang'anira kuti pangakhale wina wakuperewera chisomo cha Mulungu, kuti ungapuke muzu wina wa kuwawa mtima ungavute inu, ndipo aunyinji angadetsedwe nao;


Ndidza msanga; gwira chimene uli nacho, kuti wina angalande korona wako.