Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Timoteyo 4:4 - Buku Lopatulika

ndipo adzalubza dala pachoonadi, nadzapatukira kutsata nthano zachabe.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

ndipo adzalubza dala pachoonadi, nadzapatukira kutsata nthano zachabe.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adzafulatira choona, osafunanso kuchimva, ndipo adzangotsata nthano chabe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Sadzafuna kumva choona koma adzafuna kumva nthano chabe.

Onani mutuwo



2 Timoteyo 4:4
13 Mawu Ofanana  

Pakuti kubwerera m'mbuyo kwa achibwana kudzawapha; ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.


amene amati kwa alauli, Mtima wanu usapenye; ndi kwa aneneri, Musanenere kwa ife zinthu zoona, munene kwa ife zinthu zamyadi, munenere zonyenga;


Koma anakana kumvera, nakaniza phewa lao, natseka makutu ao, kuti asamve.


Chifukwa unalemera mtima wa anthu awa, ndipo m'makutu ao anamva mogontha, ndipo maso ao anatsinzina; kuti asaone konse ndi maso, asamve ndi makutu, asazindikire ndi mtima wao, asatembenuke, ndipo ndisawachiritse iwo.


Koma anafuula ndi mau aakulu, natseka m'makutu mwao, namgumukira iye ndi mtima umodzi;


Ndipo chifukwa chake Mulungu atumiza kwa iwo machitidwe a kusocheretsa, kuti akhulupirire bodza;


kapena asasamale nkhani zachabe, ndi mawerengedwe osalekeza a mafuko a makolo, ndiwo akuutsa mafunso, osati za udindo wa Mulungu umene uli m'chikhulupiriro;


koma nkhani zachabe ndi za akazi okalamba ukane. Ndipo udzizoloweretse kuchita chipembedzo;


Timoteo iwe, dikira chokusungitsa, ndi kulewa zokamba zopanda pake ndi zotsutsana za ichi chitchedwa chizindikiritso konama;


Ichi uchidziwa, kuti onse a mu Asiya adabwerera kusiyana nane; a iwo ali Figelo ndi Heremogene.


osasamala nthano zachabe za Chiyuda, ndi malamulo a anthu opatuka kusiyana nacho choonadi.


Chisomo chikhale ndi inu nonse, Amen.


Pakuti sitinatsate miyambi yachabe, pamene tinakudziwitsani mphamvu ndi maonekedwe a Ambuye wathu Yesu Khristu, koma tinapenya m'maso ukulu wake.