Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 23:15 - Buku Lopatulika

Ndipo Davide analakalaka nati, Ha! Wina akadandipatsa madzi a m'chitsime cha ku Betelehemu chili pachipatapo!

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Davide analakalaka nati, Ha! Wina akadandipatsa madzi a m'chitsime cha ku Betelehemu chili pachipatapo!

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono Davide adalankhula molakalaka kuti, “Ha, wina akadandipatsa madzi akumwa a m'chitsime chimene chili ku chipata ku Betelehemu kuti ndimwe!”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Davide analakalaka madzi ndipo anati, “Haa, pakanapezeka munthu wokanditungira madzi a mʼchitsime chomwe chili pafupi ndi chipata cha ku Betelehemu!”

Onani mutuwo



2 Samueli 23:15
12 Mawu Ofanana  

Ndipo anafa Rakele, naikidwa panjira ya ku Efurata (ndiwo Betelehemu).


Ndipo ngwazi zitatuzo zinapyola khamu la Afilisti, ndipo zinatunga madzi m'chitsime cha ku Betelehemu, cha pa chipatacho, nawatenga, nafika nao kwa Davide; koma iye sanafune kumwako, koma anawathira pansi kwa Yehova.


Ndipo Davide analakalaka, nati, Ha? Mwenzi wina atandimwetsa madzi a m'chitsime cha ku Betelehemu chili kuchipata.


Moyo wanga unakomoka ndi kukhumba chipulumutso chanu: Ndinayembekezera mau anu.


Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga; ndidzakufunani m'matanda kucha. Moyo wanga ukumva ludzu la kwa Inu, thupi langa lilirira Inu, m'dziko louma ndi lotopetsa, lopanda madzi.


Wosauka ndi wosowa afuna madzi, ndipo palibe, ndi lilime lao lilephera, chifukwa cha ludzu; Ine Yehova ndidzawayankha, Ine Mulungu wa Israele sindidzawasiya.


Pakuti ndidzathira madzi padziko limene lilibe madzi, ndi mitsinje pa nthaka youma; ndidzathira mzimu wanga pa mbeu yako, ndi mdalitso wanga pa obadwa ako;


Yesu anayankha nati kwa iye, Ukadadziwa mtulo wa Mulungu, ndi Iye amene alinkunena ndi iwe, Undipatse Ine ndimwe; ukadapempha Iye, ndipo akadakupatsa madzi amoyo.


koma iye wakumwa madzi amene Ine ndidzampatsa sadzamva ludzu nthawi zonse; koma madzi amene Ine ndidzampatsa adzakhala mwa iye kasupe wa madzi otumphukira kumoyo wosatha.


Koma tsiku lomaliza, lalikululo la chikondwerero, Yesu anaimirira nafuula, ndi kunena, Ngati pali munthu akumva ludzu, adze kwa Ine, namwe.