Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 22:42 - Buku Lopatulika

Anayang'ana iwo, koma panalibe wopulumutsa; ngakhale kwa Yehova, koma Iye sanawayankhe.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Anayang'ana iwo, koma panalibe wopulumutsa; ngakhale kwa Yehova, koma Iye sanawayankhe.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adakuwa, koma panalibe ndi mmodzi yemwe woŵapulumutsa. Adalirira Chauta, koma sadaŵayankhe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.

Onani mutuwo



2 Samueli 22:42
10 Mawu Ofanana  

Kodi Mulungu adzamvera kufuula kwake, ikamdzera nsautso?


Pamenepo adzandiitana, koma sindidzavomera; adzandifunatu, osandipeza ai;


Ndipo pamene mutambasula manja anu, ndidzakubisirani inu maso anga; inde pochulukitsa mapemphero anu Ine sindidzamva; manja anu adzala mwazi.


Tsiku limenelo munthu adzayang'ana kwa Mlengi wake, ndipo maso ake adzalemekeza Woyera wa Israele.


Ndipo iye sadzayang'ana pa maguwa a nsembe, ntchito ya manja ake, ngakhale kulemekeza chimene anachipanga ndi zala zake, ngakhale zifanizo pena mafano a dzuwa.


Wobadwa ndi munthu iwe lankhula ndi akulu a Israele, nunene nao, Atero Ambuye Yehova, Mwadza kodi kufunsira kwa Ine? Pali Ine, sindidzafunsidwa ndi inu, ati Ambuye Yehova.


Pamenepo adzafuulira kwa Yehova, koma sadzawayankha; inde, adzawabisira nkhope yake nthawi yomweyo, monga momwe anaipsa machitidwe ao.


Ndipo pamene Saulo anafunsira kwa Yehova, Yehova sanamyankhe ngakhale ndi maloto, kapena ndi Urimu, kapena ndi aneneri.