Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 22:33 - Buku Lopatulika

Mulungu ndiye linga langa lamphamvu; ndipo Iye ayendetsa angwiro mu njira yake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mulungu ndiye linga langa lamphamvu; ndipo Iye ayendetsa angwiro mu njira yake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mulungu wathu ndiye linga langa lolimba, wandichotsera zoopsa m'njira zanga.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.

Onani mutuwo



2 Samueli 22:33
19 Mawu Ofanana  

Ndipo anati, Yehova ndiye thanthwe langa, ndi ngaka yanga, ndi Mpulumutsi wanga, wangadi.


Kodi Wamphamvuyonse akondwera nako kuti iwe ndiwe wolungama? Kapena kodi apindula nako kuti ukwaniritsa njira zako?


Ndidzachita mwanzeru m'njira yangwiro; mudzandidzera liti? Ndidzayenda m'nyumba mwanu ndi mtima wangwiro.


Maso anga ayang'ana okhulupirika m'dziko, kuti akhale ndi Ine; iye amene ayenda m'njira yangwiro, iyeyu adzanditumikira Ine.


Odala angwiro m'mayendedwe ao, akuyenda m'chilamulo cha Yehova.


Mulungu ndiye wondizingiza mphamvu m'chuuno, nakonza njira yanga ikhale yangwiro.


Yehova ndiye kuunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndiye mphamvu ya moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?


Ine ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo; ndidzakupangira ndi diso langa lakuyang'ana iwe.


Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu, thandizo lopezekeratu m'masautso.


Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, ndipo wakhala chipulumutso changa; ameneyo ndiye Mulungu wanga, ndidzamlemekeza; ndiye Mulungu wa kholo langa, ndidzamveketsa.


usaope, pakuti Ine ndili pamodzi ndi iwe; usaopsedwe, pakuti Ine ndine Mulungu wako; ndidzakulimbitsa; inde, ndidzakuthangata; inde, ndidzakuchirikiza ndi dzanja langa lamanja la chilungamo.


Ndipo ndidzawalimbitsa mwa Yehova; ndipo adzayendayenda m'dzina lake; ati Yehova.


Ndipo ananena kwa ine, Chisomo changa chikukwanira; pakuti mphamvu yanga ithedwa mu ufooko. Chifukwa chake makamaka ndidzadzitamandira mokondweratu m'mafooko anga, kuti mphamvu ya Khristu ikhale pa ine.


Chotsalira, tadzilimbikani mwa Ambuye, ndi m'kulimba kwa mphamvu yake.


Mukhale angwiro ndi Yehova Mulungu wanu.


Ndikhoza zonse mwa Iye wondipatsa mphamvuyo.


akuyeseni inu opanda chilema m'chinthu chilichonse chabwino, kuti muchite chifuniro chake; ndi kuchita mwa ife chomkondweretsa pamaso pake, mwa Yesu Khristu; kwa Iyeyu ukhale ulemerero kunthawi za nthawi. Amen.