Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 12:28 - Buku Lopatulika

Chifukwa chake tsono musonkhanitse anthu otsalawo, nimumangire mzindawo zithando, muulande; kuti ine ndingalande mzindawo, ndipo ungatchedwe ndi dzina langa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Chifukwa chake tsono musonkhanitse anthu otsalawo, nimumangire mudziwo zithando, muulande; kuti ine ndingalande mudziwo, ndipo ungatchedwe ndi dzina langa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono inu musonkhanitse ankhondo onse otsala, ndipo bwerani mudzauzinge ndi zithando mzindawo ndi kuulanda, kuwopa kuti ine ndikalanda mzindawo, ungamatchedwe dzina langa.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo tsopano sonkhanitsani asilikali onse ndipo muzungulire mzindawo ndi kuwulanda.”

Onani mutuwo



2 Samueli 12:28
3 Mawu Ofanana  

Yowabu natumiza mithenga kwa Davide nati, Ndaponyana ndi Raba, inde ndalanda mzinda wa pamadzi.


Ndipo Davide anasonkhanitsa anthu onse, napita ku Raba, naponyana nao, naulanda.


Iye wolankhula zochokera kwa iye yekha afuna ulemu wa mwini yekha. Iye wakufuna ulemu wa Iye amene anamtuma, yemweyu ali woona, ndipo mwa Iye mulibe chosalungama.