Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




2 Samueli 12:27 - Buku Lopatulika

Yowabu natumiza mithenga kwa Davide nati, Ndaponyana ndi Raba, inde ndalanda mzinda wa pamadzi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yowabu natumiza mithenga kwa Davide nati, Ndaponyana ndi Raba, inde ndalanda mudzi wa pamadzi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Adatuma amithenga kwa Davide kukamuuza kuti, “Ndauthira nkhondo mzinda wa Raba, ndipo ndalanda nkhokwe yake ya madzi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo Yowabu anatumiza amithenga kwa Davide kukanena kuti, “Ine ndamenyana ndi Raba ndipo ndatenga zitsime zake za madzi.

Onani mutuwo



2 Samueli 12:27
5 Mawu Ofanana  

Ndipo kunali pofikanso chaka, nyengo yakutuluka mafumu, Davide anatumiza Yowabu, pamodzi ndi anyamata ake, ndi Aisraele onse; ndipo iwo anasakaza ana a Amoni, naumangira misasa yankhondo Raba. Koma Davide anatsalira ku Yerusalemu.


Ndipo Yowabu anathira nkhondo pa Raba wa ana a Amoni, nalanda mzinda wachifumu.


Chifukwa chake tsono musonkhanitse anthu otsalawo, nimumangire mzindawo zithando, muulande; kuti ine ndingalande mzindawo, ndipo ungatchedwe ndi dzina langa.


Uiike njira yodzera lupanga kunka ku Raba wa ana a Amoni, ndi ya ku Yuda ku Yerusalemu, mudzi walinga.


(Pakuti Ogi mfumu ya Basani anatsala yekha wa iwo otsalira Arefaimu; taonani, kama wake ndiye kama wachitsulo; sukhala kodi mu Raba wa ana a Amoni? Utali wake mikono isanu ndi inai, kupingasa kwake mikono inai, kuyesa mkono wa munthu).