2 Akorinto 3:10 - Buku Lopatulika Pakutinso chimene chinachitidwa cha ulemerero sichinachitidwe cha ulemerero m'menemo, chifukwa cha ulemerero woposawo. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Pakutinso chimene chinachitidwa cha ulemerero sichinachitidwa cha ulemerero m'menemo, chifukwa cha ulemerero woposawo. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Chifukwa cha ulemerero wopambanawu umene waoneka tsopano, zinthu zimene kale zidaali ndi ulemerero, masiku ano zilibenso ulemerero konse. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Pakuti zimene zinali ndi ulemerero, tsopano zilibenso ulemerero pofananitsa ndi ulemerero wopambanawo. |
Pompo mwezi udzanyazitsidwa, ndi dzuwa lidzakhala ndi manyazi, pakuti Yehova wa makamu adzalamulira chaulemerero m'phiri la Ziyoni, ndi mu Yerusalemu, ndi pamaso pa akuluakulu ake.
Adatsala ndani mwa inu amene anaona nyumba iyi mu ulemerero wake woyamba? Ndipo muiona yotani tsopano? Kodi siikhala m'maso mwanu ngati chabe?
dzuwa lamsana, ndinaona panjira, Mfumu, kuunika kochokera kumwamba kowalitsa koposa dzuwa kunawala pondizinga ine ndi iwo akundiperekeza.
Pakuti ngati chimene chilikuchotsedwa chinakhala mu ulemerero, makamaka kwambiri chotsalacho chili mu ulemerero.
Pakuti ngati utumiki wa chitsutso unali wa ulemerero, makamaka utumiki wa chilungamo uchulukira muulemerero kwambiri.
Pakuti analandira kwa Mulungu Atate ulemu ndi ulemerero, pakumdzera Iye mau otere ochokera ku ulemerero waukulu, Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa, amene Ine ndikondwera naye;
Ndipo sikudzakhalanso usiku; ndipo sasowa kuunika kwa nyali, ndi kuunika kwa dzuwa; chifukwa Ambuye Mulungu adzawaunikira; ndipo adzachita ufumu kunthawi za nthawi.