Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 30:11 - Buku Lopatulika

Ndipo ena anapeza Mwejipito kuthengo, nabwera naye kwa Davide, nampatsa chakudya, nadya iye; nampatsanso madzi kumwa;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo ena anapeza Mwejipito kuthengo, nabwera naye kwa Davide, nampatsa chakudya, nadya iye; nampatsanso madzi kumwa;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Anthu amene anali ndi Davide, akuyenda m'njira, adapeza Mwejipito, nabwera naye kwa Davide. Tsono adampatsa buledi naadya. Adampatsanso madzi akumwa,

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Anthu amene anali ndi Davide anapeza Mwigupto mʼmunda wina ndipo anabwera naye kwa Davide. Iwo anamupatsa madzi kuti amwe ndi chakudya kuti adye.

Onani mutuwo



1 Samueli 30:11
9 Mawu Ofanana  

Mdani wako akamva njala umdyetse, akamva ludzu ummwetse madzi.


pakuti ndinali ndi njala, ndipo munandipatsa Ine kudya; ndinali ndi ludzu, ndipo munandimwetsa Ine; ndinali mlendo, ndipo munachereza Ine;


Musamanyansidwa naye Mwedomu, popeza ndiye mbale wanu; musamanyansidwa naye Mwejipito, popeza munali alendo m'dziko lake.


Ana obadwa nao a mbadwo wachitatu alowe m'msonkhano wa Yehova.


Ndipo Davide anawalondola, iye ndi anthu mazana anai; koma anthu mazana awiri anatsala m'mbuyo, chifukwa analema, osakhoza kuoloka kamtsinje Besori.


nampatsanso chigamphu cha nchinchi ya nkhuyu ndi nchinchi ziwiri za mphesa; ndipo atadya, moyo wake unabweranso mwa iye; pakuti adagona masiku atatu ndi usiku wao, osadya chakudya, osamwa madzi.