Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 29:5 - Buku Lopatulika

Uyu si Davide kodi amene anamthirirana mang'ombe m'magulu ao, kuti, Saulo anapha zikwi zake, koma Davide zikwi zake zankhani?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Uyu si Davide kodi amene anamthirirana mang'ombe m'magulu ao, kuti, Saulo anapha zikwi zake, koma Davide zikwi zake zankhani?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ameneyutu ndi Davide, yemwe uja ankamuvinira ndi kumuimbira kuti, “ ‘Saulo wapha zikwi inde, koma Davide wapha zikwi khumikhumi?’ ”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti, “ ‘Sauli wapha anthu 1,000 koma Davide wapha miyandamiyanda?’ ”

Onani mutuwo



1 Samueli 29:5
4 Mawu Ofanana  

Ndipo Miriyamu mneneriyo, mlongo wa Aroni, anagwira lingaka m'dzanja lake; ndipo akazi onse anatuluka kumtsata ndi malingaka ndi kuthira mang'ombe.


Yemwe adalitsa mnzake ndi mau aakulu pouka mamawa, anthu adzachiyesa chimenecho temberero.


Ndipo anyamata a Akisi ananena naye, Uyu si Davide mfumu ya dzikolo kodi? Sanathirirana mang'ombe za iye kodi m'magule ao, ndi kuti, Saulo anapha zikwi zake, koma Davide zikwi zake zankhani?