Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 28:5 - Buku Lopatulika

Ndipo pamene Saulo anaona khamu la Afilisti, anaopa, ndi mtima wake unanjenjemera kwakukulu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo pamene Saulo anaona khamu la Afilisti, anaopa, ndi mtima wake unanjenjemera kwakukulu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Saulo ataona gulu laankhondo la Afilisti, adayamba kuwopa ndi kunjenjemera kwambiri.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Sauli ataona gulu lankhondo la Afilisti anaopa ndipo ananjenjemera kwambiri.

Onani mutuwo



1 Samueli 28:5
11 Mawu Ofanana  

M'makutu mwake mumveka zoopsetsa; pali mtendere amfikira wakumuononga.


Zoopetsa zidzamchititsa mantha monsemo, nadzampirikitsa kumbuyo kwake.


Ha? M'kamphindi ayesedwa bwinja; athedwa konse ndi zoopsa.


Chomwe woipa achiopa chidzamfikira; koma chomwe olungama achifuna chidzapatsidwa.


Ndipo anauza a nyumba ya Davide, kuti Aramu wapangana ndi Efuremu. Ndipo mtima wake unagwedezeka, ndi mtima wa anthu ake, monga mitengo ya m'nkhalango igwedezeka ndi mphepo.


Pamenepo padasandulika pa nkhope pake pa mfumu, ndi maganizo ake anamsautsa, ndi mfundo za m'chuuno mwake zinaguluka, ndi maondo ake anaombana.


Ndipo Afilisti anasonkhana, nadza namanga misasa ku Sunemu; ndipo Saulo anasonkhanitsa Aisraele onse, namanga iwo ku Gilibowa.


Ndipo pamene Saulo anafunsira kwa Yehova, Yehova sanamyankhe ngakhale ndi maloto, kapena ndi Urimu, kapena ndi aneneri.