Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 28:20 - Buku Lopatulika

Pomwepo Saulo anagwa pansi tantha, naopa kwakukulu, chifukwa cha mau a Samuele; ndipo analibe mphamvu; pakuti tsiku lonse ndi usiku wake wonse anakhala osadya kanthu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pomwepo Saulo anagwa pansi tantha, naopa kwakukulu, chifukwa cha mau a Samuele; ndipo analibe mphamvu; pakuti tsiku lonse ndi usiku wake wonse anakhala osadya kanthu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pompo Saulo adagwa pansi, kuchita kuti nyutu, ali wodzazidwa ndi mantha chifukwa cha mau a Samuele. Ndipo analibenso nyonga, poti sadadye kanthu tsiku lonse.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nthawi yomweyo Sauli anagwa pansi atadzazidwa ndi mantha chifukwa cha mawu a Samueli. Analibenso mphamvu, pakuti sanadye tsiku lonse.

Onani mutuwo



1 Samueli 28:20
7 Mawu Ofanana  

Wamthandiza bwanji wopanda mphamvu. Kulipulumutsa dzanja losalimba!


Tsono m'mawa vinyo atamchokera Nabala, mkazi wake anamuuza zimenezi; ndipo mtima wake unamyuka m'kati mwake, iye nasanduka ngati mwala.


Ndiponso Yehova adzapereka Israele pamodzi ndi iwe m'dzanja la Afilisti; ndipo mawa iwe ndi ana ako mudzakhala kuli ine; Yehova adzaperekanso khamu la Aisraele m'dzanja la Afilisti.


Ndipo mkaziyo anafika kwa Saulo, naona kuti ali wovutika kwambiri, nanena naye, Onani, mdzakazi wanu anamvera mau anu, ndipo ndinataya moyo wanga, ndi kumvera mau anu munalankhula ndi ine.


Ndipo pamene Saulo anaona khamu la Afilisti, anaopa, ndi mtima wake unanjenjemera kwakukulu.