Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 20:19 - Buku Lopatulika

Ndipo atapita masiku atatu, utsike msanga, nufike kumene unabisala tsiku la mlandu uja, nukhale pamwala wa Ezeri.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo atapita masiku atatu, utsike msanga, nufike kumene unabisala tsiku la mlandu uja, nukhale pa mwala wa Ezeri.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mkucha adzakufunanso kwambiri. Tsono udzapite ku malo amene udaabisala tsiku lijali, ndipo ukakhale pa mbali ina ya mulu wa miyala uli apowo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mkuja adzakufunafuna. Tsono udzapite pamalo pamene unabisala poyamba paja ndipo ukadikire pa mulu wa miyala uli apowo.

Onani mutuwo



1 Samueli 20:19
6 Mawu Ofanana  

Ndipo Saulo analankhula kwa Yonatani mwana wake, ndi anyamata ake onse kuti amuphe Davide.


Koma Yonatani mwana wa Saulo anakondwera kwambiri ndi Davide. Ndipo Yonatani anauza Davide, nati, Saulo atate wanga alikufuna kukupha; chifukwa chake tsono uchenjere m'mawa, mukhale m'malo mosadziwika, nubisale;


Tsono Yonatani ananena kwa Davide, Mawa mwezi ukhala; ndipo adzakufuna, popeza udzasoweka pamalo pako.


Ndipo ine ndidzaponya mivi itatu pambali pake, monga ngati ndilikuponya pachandamali.


Ndipo m'mawa, Yonatani ananka kuthengoko pa nthawi imene anapangana ndi Davide, ali ndi kamnyamata.


Nati Davide kwa Yonatani, Onani, mawa mwezi ukhala, ndipo ine ndiyenera kupita kukadya kwa mfumu, wosatsala; koma undilole ndikabisale kuthengo, kufikira tsiku lachitatu madzulo ake.