Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 14:32 - Buku Lopatulika

Ndipo anthuwo anathamangira zowawanyazo, natenga nkhosa, ndi ng'ombe, ndi anaang'ombe, naziphera pansi; anthu nazidya zili ndi mwazi wao.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anthuwo anathamangira zowawanyazo, natenga nkhosa, ndi ng'ombe, ndi anaang'ombe, naziphera pansi; anthu nazidya zili ndi mwazi wao.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Motero adathamangira pa zofunkha, ndipo adatenga nkhosa, ng'ombe ndi makonyani, nazipha. Ndipo adazidya pamodzi ndi magazi omwe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Choncho iwo anathamangira pa zofunkha ndipo anatenga nkhosa, ngʼombe ndi ana angʼombe. Iwo anazipha zonsezi nazidya pamodzi ndi magazi omwe.

Onani mutuwo



1 Samueli 14:32
11 Mawu Ofanana  

Koma nyama, m'mene muli moyo wake, ndiwo mwazi wake, musadye.


Chifukwa chake unene nao, Atero Ambuye Yehova, Mumadyera kumodzi ndi mwazi, mumakwezera maso anu kumafano anu, ndi kukhetsa mwazi; ndipo kodi mudzakhala nalo dziko cholowa chanu?


Musamadya kanthu ndi mwazi wake; musamachita nyanga, kapena kuombeza ula.


Likhale lemba losatha m'mibadwo yanu m'nyumba zanu zonse, musamadya kapena mafuta kapena mwazi.


koma kuti tilembere kwa iwo, kuti asale zonyansa za mafano, ndi dama, ndi zopotola, ndi mwazi.


kuti musale nsembe za mafano, ndi mwazi, ndi zopotola, ndi dama; ngati mudzisungitsa pa zimenezi, kudzakhala bwino kwa inu. Tsalani bwino.


Mwazi wao wokha musamadya; muziuthira panthaka ngati madzi.


Chifukwa ninji tsono simunamvere mau a Yehova, koma munathamangira zowawanya, ndi kuchita choipa pamaso pa Yehova?