Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Samueli 14:25 - Buku Lopatulika

Ndipo anthu onsewo analowa munkhalango, panali uchi pansi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo anthu onsewo analowa munkhalango, panali uchi pansi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono onse adaloŵa m'nkhalango ina m'mene munali uchi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Gulu lonse la ankhondo linalowa mʼnkhalango mmene munali uchi.

Onani mutuwo



1 Samueli 14:25
8 Mawu Ofanana  

ndipo ndatsikira kuwalanditsa m'manja a anthu a Ejipito, ndi kuwatulutsa m'dziko lija akwere nalowe m'dziko labwino ndi lalikulu, m'dziko moyenda mkaka ndi uchi ngati madzi; ku malo a Akanani, ndi Ahiti, ndi Aamori, ndi Aperizi, ndi Ahivi, ndi Ayebusi.


Wapeza uchi kodi? Idyapo wokwanira, kuti ungakukole, nusanze.


Ndipo anafotokozera, nati Tinakafika ku dziko limene munatitumirako, ndilo ndithu moyenda mkaka ndi uchi ngati madzi; ndi zipatso zake siizi.


kuti linganene dziko limene mudatitulutsako, Popeza Yehova sanakhoze kuwalowetsa m'dziko limene adanena nao, ndi popeza anadana nao, anawatulutsa kuti awaphe m'chipululu.


Ndipo anaufula ndi dzanja lake, nayenda, namadya alimkuyenda, nadza kwa atate wake ndi amai wake, nawapatsa, nadya iwo; koma sanawauze kuti adaufula uchiwo m'chitanda cha mkango.


Ndipo Aisraele anasauka tsiku lija; pakuti Saulo anawalumbirira, kuti, Atembereredwe iye wakudya kanthu kufikira madzulo, ndikabwezere chilango adani anga. Motero anthu onse anakhala opanda kudya.


Ndipo pakufika anthuwo m'nkhalangomo, onani, madzi a uchi anachuluka; koma panalibe munthu mmodzi anaika dzanja lake pakamwa, pakuti anthuwo anaopa tembererolo.