Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Akorinto 9:11 - Buku Lopatulika

Ngati takufeserani inu zauzimu, kodi nchachikulu ngati ife tituta za thupi lanu?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ngati takufeserani inu zauzimu, kodi nchachikulu ngati ife tituta za thupi lanu?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ngati ife tidafesa zabwino zauzimu pakati panu, nanga tilekerenji kulandira kwa inu zotisoŵa m'moyo wathu wathupi?

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ngati tidzala mbewu yauzimu pakati panu, kodi ndi chovuta kwambiri kuti tikolole zosowa zathu kuchokera kwa inu?

Onani mutuwo



1 Akorinto 9:11
8 Mawu Ofanana  

Pamenepo anyamata ake anasendera, nanena naye, nati, Atate wanga, mneneri akadakuuzani chinthu chachikulu, simukadachichita kodi? Koposa kotani nanga ponena iye, Samba, nukonzeke?


kapena thumba la kamba la kunjira, kapena malaya awiri, kapena nsapato, kapena ndodo; pakuti wantchito ayenera kulandira zakudya zake.


Pakuti kunakondweretsa iwo; ndiponso iwo ali amangawa ao. Pakuti ngati amitundu anagawana zinthu zao zauzimu, alinso amangawa akutumikira iwo ndi zinthu zathupi.


Chomwechonso Ambuye analamulira kuti iwo amene alalikira Uthenga Wabwino akhale ndi moyo ndi Uthenga Wabwino.


Chifukwa chake sikuli kanthu kwakukulu ngatinso atumiki ake adzionetsa monga atumiki a chilungamo; amene chimaliziro chao chidzakhala monga ntchito zao.


Koma iye amene aphunzira mau, ayenera kuchereza womphunzitsayo m'zonse zabwino.


Sikunena kuti nditsata choperekacho, komatu nditsata chipatso chakuchulukira ku chiwerengero chanu.