Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Akorinto 7:6 - Buku Lopatulika

Koma ichi ndinena monga mwa kulola, si monga mwa kulamulira.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma ichi ndinena monga mwa kulola, si monga mwa kulamulira.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pamene ndikunena zimenezi, sindikuchita mokulamulani ai, koma mokulolani chabe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndikunena zimenezi mokulolani chabe osati mokulamulani.

Onani mutuwo



1 Akorinto 7:6
6 Mawu Ofanana  

Koma okwatitsidwawo ndiwalamulira, si ine ai, koma Ambuye, kuti mkazi asasiye mwamuna,


Koma kwa otsalawo ndinena ine, si Ambuye, Ngati mbale wina ali naye mkazi wosakhulupirira, ndipo iye avomera mtima kukhala naye pamodzi, asalekane naye.


Koma kunena za anamwali, ndilibe lamulo la Ambuye; koma ndikuuzani choyesa iye, monga wolandira chifundo kwa Ambuye kukhala wokhulupirika.


Koma akhala wokondwera koposa ngati akhala monga momwe ali, monga mwa kuyesa kwanga; ndipo ndinagiza kuti inenso ndili naye Mzimu wa Mulungu.


Chimene ndilankhula sindilankhula monga mwa Ambuye, koma monga wopanda nzeru, m'kulimbika kumene kwa kudzitamandira.


Sindinena ichi monga kulamulira, koma kuyesa mwa khama la ena choonadi cha chikondi chanunso.