Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Akorinto 5:12 - Buku Lopatulika

Pakuti nditani nao akunja kukaweruza iwo? Kodi amene ali m'katimo simuwaweruze ndi inu,

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti nditani nao akunja kukaweruza iwo? Kodi amene ali m'katimo simuwaweruza ndi inu,

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nanga kuweruza anthu amene adakali kunja, ndi ntchito yanga ngati? Si koma amene ali mu mpingo ndiwo muyenera kuŵaweruza?

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kodi ndipindulanji kuti ndiweruze anthu amene si a mu mpingo? Kodi simuyenera kuweruza iwo amene ali mu mpingo?

Onani mutuwo



1 Akorinto 5:12
8 Mawu Ofanana  

Ndipo Iye ananena nao, Kwa inu kwapatsidwa chinsinsi cha Ufumu wa Mulungu; koma kwa iwo ali kunja zonse zichitidwa m'mafanizo;


Koma anati kwa iye, Munthu iwe, ndani anandiika Ine ndikhale woweruza, kapena wakugawira inu?


Yesu anayankha, Ufumu wanga suli wa dziko lino lapansi; ufumu wanga ukadakhala wa dziko lino lapansi, anyamata anga akadalimbika nkhondo, kuti ndisaperekedwe kwa Ayuda; koma tsopano ufumu wanga suli wochokera konkuno.


Muyendere munzeru ndi iwo akunja, kuchita machawi nthawi ingatayike.


kuti mukayende oona mtima pa iwo a kunja, ndi kukhala osasowa kanthu.


Kuyeneranso kuti iwo akunja adzakhoza kumchitira umboni wabwino; kuti ungamgwere mtonzo, ndi msampha wa mdierekezi.