Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Akorinto 4:18 - Buku Lopatulika

Koma ena adzitukumula, monga ngati sindinalinkudza kwa inu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma ena adzitukumula, monga ngati sindinalinkudza kwa inu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ena mwayamba kudzitukumula, monga ngati sindidzabwerako kwanu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ena mwa inu mukudzitukumula, ngati kuti sindingabwere kwanu.

Onani mutuwo



1 Akorinto 4:18
5 Mawu Ofanana  

Kodi ndifike kwa inu ndi ndodo, kapena mwachikondi, ndi mzimu wakufatsa?


Ndipo mukhala odzitukumula, kosati makamaka mwachita chisoni, kuti achotsedwe pakati pa inu iye amene anachita ntchito iyi.


koma ndipempha kuti pokhala ndili pomwepo, ndisalimbike mtima ndi kulimbika kumene ndiyesa kulimbika nako pa ena, amene atiyesera ife monga ngati tilikuyendayenda monga mwa thupi.


Pakuti ndiopa, kuti kaya, pakudza ine, sindidzakupezani inu otere onga ndifuna, ndipo ine ndidzapezedwa ndi inu wotere wonga simufuna; kuti kaya pangakhale chotetana, kaduka, mikwiyo, zilekanitso, maugogodi, ukazitape, zodzikuza, mapokoso;