Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Akorinto 15:8 - Buku Lopatulika

ndipo potsiriza pake pa onse, anaoneka kwa inenso monga mtayo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

ndipo potsiriza pake pa onse, anaoneka kwa inenso monga mtayo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Potsiriza, pambuyo pa onse adandiwonekeranso ineyo, ngakhale ndili ngati mpolo chabe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Potsiriza pa onse anaonekeranso kwa ine, monga mwana wobadwa nthawi isanakwane.

Onani mutuwo



1 Akorinto 15:8
10 Mawu Ofanana  

Ndipo Ambuye anati kwa Paulo usiku m'masomphenya, Usaope, koma nena, usakhale chete;


Ndipo anati, Mulungu wa makolo athu anakusankhiratu udziwe chifuniro chake, nuone Wolungamayo, numve mau otuluka m'kamwa mwake.


ndipo ndinamuona Iye, nanena nane, Fulumira, tuluka msanga mu Yerusalemu; popeza sadzalandira umboni wako wakunena za Ine.


Ndipo kunali, pakupita ine ndi kuyandikira ku Damasiko, monga usana, mwadzidzidzi kunandiwalira pondizungulira ine kuunika kwakukulu kochokera kumwamba.


M'menemo popita ine ku Damasiko ndi ulamuliro ndi ukumu wa kwa ansembe aakulu,


Komatu uka, imirira pa mapazi ako; pakuti chifukwa cha ichi ndinaonekera kwa iwe, kukuika iwe ukhale mtumiki ndi mboni ya izi wandionamo Ine, ndiponso ya izi ndidzakuonekeramo iwe;


Ndipo anachoka Ananiya, nalowa m'nyumbayo; ndipo anaika manja ake pa iye, nati, Saulo, mbale, Ambuye wandituma ine, ndiye Yesu amene anakuonekerani panjira wadzerayo, kuti upenyenso, ndi kudzazidwa ndi Mzimu Woyera.


Kodi sindine mfulu? Kodi sindine mtumwi? Kodi sindinaone Yesu Ambuye wathu? Kodi simuli inu ntchito yanga mwa Ambuye?