Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Akorinto 15:12 - Buku Lopatulika

Koma ngati Khristu alalikidwa kuti waukitsidwa kwa akufa, nanga ena mwa inu anena bwanji kuti kulibe kuuka kwa akufa?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma ngati Khristu alalikidwa kuti waukitsidwa kwa akufa, nanga ena mwa inu anena bwanji kuti kulibe kuuka kwa akufa?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono popeza kuti chimene timalalika ndi chakuti Khristu adauka kwa akufa, bwanji ena mwa inu akunena kuti, “Anthu akufa sadzaukanso?”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma ngati timalalikira kuti Khristu anaukitsidwa kwa akufa, zikutheka bwanji kuti ena mwa inu azinena kuti kulibe kuuka kwa akufa?

Onani mutuwo



1 Akorinto 15:12
7 Mawu Ofanana  

Ndipo pamene anamva za kuuka kwa akufa ena anaseka pwepwete; koma ena anati, Tidzakumvanso za chimenechi.


Pakutitu Asaduki anena kuti kulibe kuuka kwa akufa, kapena mngelo, kapena mzimu; koma Afarisi avomereza ponse pawiri.


Muchiyesa chinthu chosakhulupirika, chakuti Mulungu aukitsa akufa?


Ngati ine tsono, kapena iwowa, kotero tilalikira, ndi kotero munakhulupirira.


asangalatse mitima yanu, nakhazikitse inu mu ntchito yonse ndi mau onse abwino.


ndiwo amene adasokera kunena za choonadi, ponena kuti kuuka kwa akufa kwachitika kale, napasula chikhulupiriro cha ena.