Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Akorinto 14:8 - Buku Lopatulika

Pakuti ngati lipenga lipereka mau osazindikirika, adzadzikonzera ndani kunkhondo?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti ngati lipenga lipereka mau osazindikirika, adzadzikonzera ndani kunkhondo?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndiponso woliza lipenga akapanda kuliliza momveka bwino, ndani angakonzekere nkhondo?

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Komanso ngati lipenga silimveka bwino, ndani angakonzekere nkhondo?

Onani mutuwo



1 Akorinto 14:8
12 Mawu Ofanana  

Ndipo padzakhala tsiku limenelo, lipenga lalikulu lidzaombedwa; ndipo adzafika omwe akadatayika m'dziko la Asiriya, ndi opirikitsidwa a m'dziko la Ejipito; ndipo adzapembedza Yehova m'phiri lopatulika la pa Yerusalemu.


Matumbo anga, matumbo anga! Ndipoteka pamtima panga penipeni; mtima wanga sukhala pansi m'kati mwanga; sindithai kutonthola; pakuti wamva, moyo wanga, mau a lipenga, mbiri ya nkhondo.


Muombe lipenga mu Ziyoni, nimufuulitse m'phiri langa lopatulika; onse okhala m'dziko anjenjemere; pakuti tsiku la Yehova lilinkudza, pakuti liyandikira;


Kodi adzaomba lipenga m'mzinda osanjenjemera anthu? Kodi choipa chidzagwera mzinda osachichita Yehova?


Ndipo pamene mupita kunkhondo m'dziko lanu kuchita nkhondo pa mdani wakusautsa inu, mulize chokweza ndi malipenga; ndipo Yehova Mulungu wanu adzakumbukira inu, nadzakupulumutsani kwa adani anu.


Ngakhale zinthu zopanda moyo, zopereka mau, ngati chitoliro, kapena ngoli, ngati sizisiyanitsa maliridwe, chidzazindikirika bwanji chimene chiombedwa kapena kuimbidwa?