Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Akorinto 12:4 - Buku Lopatulika

Ndipo pali mphatso zosiyana, koma Mzimu yemweyo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo pali mphatso zosiyana, koma Mzimu yemweyo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsonotu pali mphatso zamitundumitundu, koma wozipereka ndi Mzimu Woyera mmodzimodzi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pali mphatso zosiyanasiyana, koma Mzimu yemweyo.

Onani mutuwo



1 Akorinto 12:4
11 Mawu Ofanana  

ndipo ndamdzaza ndi mzimu wa Mulungu, ndi luso, ndi nzeru, ndi chidziwitso, ndi m'ntchito zilizonse,


Koma za mphatso zauzimu, abale, sindifuna kuti mukhale osadziwa.


Ndipotu Mulungu anaika ena mu Mpingo, poyamba atumwi, achiwiri aneneri, achitatu aphunzitsi, pamenepo zozizwa, pomwepo mphatso za machiritso, mathandizo, maweruziro, malilime a mitundumitundu.


Ndipo pali mautumiki osiyana, koma Ambuye yemweyo.


Koma mwenzi anthu onse akadakhala monga momwe ndili ine ndekha. Koma munthu yense ali nayo mphatso yake ya iye yekha kwa Mulungu, wina chakuti, wina chakuti.


Ndipo Iye anapatsa ena akhale atumwi; ndi ena aneneri; ndi ena alaliki; ndi ena abusa, ndi ena aphunzitsi;


pochita umboni pamodzi nao Mulungunso ndi zizindikiro, ndi zozizwitsa ndi mphamvu za mitundumitundu ndi zogawira za Mzimu Woyera, monga mwa chifuniro chake.


monga yense walandira mphatso, mutumikirane nayo, ngati adindo okoma a chisomo cha mitundumitundu cha Mulungu;